Kadzidzi odabwitsa wagwidwa m’nyumba atanyamula ma kalataÂ

Zimbabwe News Update

🇿🇼 Published: 02 June 2026
📘 Source: Malawi 24

Zina ukamva kamba anga Mwala, zaphelezera m’boma la Nkhotakota pomwe anthu agwira Kadzidzi wa chilendo mnyumba atanyamula Kalata za uthenga othetsa banja m’mudzi mwa Phangwa m’bomalo. Malinga ndi uthenga omwe tapeza ati Kadzidziyo anapezeka atanyamula kalata ziwiri zonyamula uthenga opita kwa Mayi wa m’nyumbamo. Uthenga wa mkalatazo watsindika kuti banja lithe ponena kuti mkazi wa bambo wa mnyumbamo amulekele mwamuna wake, yemwe dzina lake ndi Thom.

kadzidziyo anasenza uthenga wa chidule kuti “Undipatse mwamuna wanga” komanso kalata ina yati “Iwe Thom ndabwera ine, tiye tidzipita ntchito tikugwilira limodzi.” zomwe zachitikazi zazizilitsa anthu nkhongono ponena kuti zifukwa za zodabwitsazi sizikudziwika ndipo apolisi akwanitsa kunyamula kadzidziyo limodzi ndi makalata omwe anali nawo komanso kukhazikitsa bata mderalo. Paul Malimwe, mneneli wa apolisi m’boma la Nkhotakota sadayankhulebe pa nkhaniyi.

📖 Continue Reading
This is a preview of the full article. To read the complete story, click the button below.

Read Full Article on Malawi 24

AllZimNews aggregates content from various trusted sources to keep you informed.

📰 Article Attribution
Originally published by Malawi 24 • June 02, 2026

Powered by
AllZimNews

All Zim News – Bringing you the latest news and updates.

By Hope